Mawu a M'munsi
c Ayuda komanso anthu amitundu ina ankakhulupirira kuti kulavula malovu ndi njira kapena chizindikiro cha kuchiritsa, ndipo mabuku a Arabi amafotokozanso za kuchiritsa pogwiritsa ntchito njirayi. Mwina Yesu analavula malovu pongofuna kuuza munthuyu kuti anali atatsala pang’ono kumuchiritsa. Koma sikuti anagwiritsa ntchito malovu ake ngati mankhwala.