Mawu a M'munsi
a Anthu ena akale omwe ankakopera Baibulo otchedwa Asoferimu anasintha vesili kuti lizimveka ngati Yeremiya ndi amene akuwerama osati Yehova. Zikuoneka kuti iwo ankaganiza kuti n’zosayenera kunena kuti Mulungu angachite zinthu modzichepetsa chonchi kuti athandize munthu. Chifukwa cha zimenezi, Mabaibulo ambiri sanamasulire bwino mfundo yosangalatsa imene ili m’vesili. Komabe, Baibulo lina linamasulira molondola kuti Yeremiya anauza Mulungu kuti: “Kumbukirani, kumbukirani ndipo mundiweramire.”—The New English Bible.