Mawu a M'munsi
a Malamulo a Arabi ankanena kuti munthu azitalikirana ndi wakhate pafupifupi mamita awiri. Ndipo ngati kukuwomba mphepo, wakhate ankafunika kutalikirana ndi anthu pafupifupi mamita 45. Buku lina limanena za Rabi wina yemwe ankabisala akaona akhate ndiponso wina amene ankawathamangitsa powagenda ndi miyala. (Midrash Rabbah) Choncho anthu akhate ankadziwa mmene zimapwetekera ukamakanidwa, kunyozedwa komanso kuona kuti anthu sakukufuna.