Mawu a M'munsi
a Mwachitsanzo, pofunsa chifukwa chimene Myudayo ankalankhulira ndi Msamariya, mayiyo anayambitsa nkhani yokhudza chidani cha kalekale pakati pa anthu a mitundu iwiriyi. (Yohane 4:9) Iye ananenanso zoti Asamariya ndi mbadwa za Yakobo, mfundo imene Ayuda ankakanitsitsa kwa mtu wagalu. (Yohane 4:12) Ayuda ankawanena Asamariya kuti ndi Akuta, pofuna kutsindika mfundo yakuti iwo si mbadwa za Yakobo, koma ndi anthu amene anachokera kwa anthu a mitundu ina.