Mawu a M'munsi
c Chaka chilichonse, Ayuda ankafunika kukhoma msonkho wa pakachisi wa ndalama zokwana madalakima awiri, ndipo ndalamazi zinkakwana pafupifupi malipiro a ntchito ya masiku awiri. Buku lina limati: “Ndalama za msonkhozi kwenikweni ankazigwiritsa ntchito polipirira zinthu zofunika popereka nsembe yopsereza imene inkaperekedwa tsiku ndi tsiku komanso nsembe zonse zimene ankaperekera anthu onse.”