Mawu a M'munsi
a Anthu ena amati mawu a Chigiriki amene anawamasulira kuti “atagwidwa ndi chifundo,” ndi ena mwa mawu amphamvu kwambiri m’Chigiriki osonyeza kumvera ena chisoni. Buku lina limati mawu amenewa “samangosonyeza kumva chisoni kokha ukaona anthu amene akuvutika, koma amatanthauzanso kukhala ndi mtima wofunitsitsa kuwathandiza komanso kuthetsa mavuto awo.”