Mawu a M'munsi
e Imeneyi sinali nthawi yokhayo imene panabatizidwa anthu ambiri. Pa 7 August 1993, anthu 7,402 anabatizidwa tsiku limodzi pamsonkhano wa mayiko wa Mboni za Yehova umene unachitika mumzinda wa Kiev m’dziko la Ukraine. Anthuwo anabatizidwa m’madamu 6 ndipo ubatizo wonse unachitika kwa maola awiri ndi 15 minitsi.