Mawu a M'munsi
b Mwina Ayuda sanaloledwe kukhala ndi sunagoge mumzindawo chifukwa chakuti munali asilikali ambiri. Kapena mwinanso amuna a Chiyuda amene anali mumzindawo anali osakwana 10, chiwerengero cha amuna amene ankafunikira kuti mumzinda mukhazikitsidwe sunagoge.