Mawu a M'munsi
d Ena amanena kuti Paulo anali ndi vuto la maso limene linamulepheretsa kuzindikira mkulu wa ansembe. Kapena mwina panali patadutsa nthawi yaitali kwambiri atachoka ku Yerusalemu moti mkulu wa ansembe amene analipo pa nthawiyo sankamudziwa. Kapenanso Paulo sanathe kuona bwinobwino munthu amene analamula kuti iye amenyedwe chifukwa panali anthu ambiri.