Mawu a M'munsi
a N’zochititsa chidwi kuti Yona anachokera m’tauni ya ku Galileya chifukwa choti, ponyoza Yesu, Afarisi ananena kuti: “Fufuza ndipo sudzapeza pamene pamati m’Galileya mudzatuluka mneneri.” (Yoh. 7:52) Omasulira mabuku ndiponso ofufuza ambiri amati ponena mawu amenewa, Afarisi ankatanthauza kuti m’mbuyomo kapena pa nthawiyi panalibiretu mneneri aliyense amene anachokera m’chigawo chonyozeka cha Galileya. Ngati izi n’zimenedi Afarisiwo ankatanthauza, ndiye kuti iwo ankanena zinthu zotsutsana ndi mbiri komanso ulosi wa m’Baibulo.—Yes. 9:1, 2.