Mawu a M'munsi
c Mawu achiheberi amene anawamasulira kuti “nsomba,” m’Chigiriki anawamasulira kuti “chilombo cha m’nyanja,” kapena kuti “chinsomba chachikulu.” Ngakhale kuti sitikudziwa kuti imeneyi inali nsomba yanji, komabe tikudziwa kuti m’nyanja ya Mediterranean muli nsomba zikuluzikulu zamtundu wa shaki zimene zingathe kumeza munthu wathunthu. M’nyanja zina nsomba zimenezi zimatha kukula kwambiri moti zina zimakhala zazitali mamita 15, kapenanso kuposa.