Mawu a M'munsi
a Mafupa amene Ezekieli anaona m’masomphenyawo sanali a anthu amene anafa chifukwa cha matenda koma a ‘anthu amene anachita kuphedwa.’ (Ezek. 37:9) “Nyumba yonse ya Isiraeli” inaphedwadi mophiphiritsa pamene anthu okhala mu ufumu wa mafuko 10 wa Isiraeli komanso anthu okhala mu ufumu wa mafuko awiri wa Yuda anagonjetsedwa ndi Asuri komanso Ababulo n’kutengedwa kupita ku ukapolo.