Mawu a M'munsi
b Akatswiri ena oikira ndemanga pa mawu a m’Baibulo, amaona kuti imeneyi ndi nkhani yabwino. Amanena kuti kwa nthawi yaitali kukumba mchere n’kumaugwiritsa ntchito poteteza zinthu kuti zisawonongeke inali bizinesi yaikulu ku Nyanja Yakufa. Koma mungaone kuti nkhaniyi ikunena mosapita m’mbali kuti madambo amenewo “sadzasintha nʼkukhala abwino.” Iwo adzakhala opanda moyo komanso sadzachiritsidwa chifukwa chakuti madzi opatsa moyo ochokera kunyumba ya Yehova sadzafika kumeneko. Choncho zikuoneka kuti pamene lembali likunena kuti madambowo adzakhala amchere, zikutanthauza kuti sadzakhala malo abwino.—Sal. 107:33, 34; Yer. 17:6.