Mawu a M'munsi
a Satana anatsogoza Hava kukhulupirira kuti mwa kuthupi iye sakafa nkomwe. (Genesis 3:1-5) Chotero sichinali kufikira pambuyo pake pamene iye anayambitsa chiphunzitso chonyenga chakuti anthu ali ndi moyo wosafa womwe umapitirizabe kukhala ndi moyo pambuyo pa imfa ya thupi.—Onani Nsanja ya Olonda, September 15, 1957, tsamba 575 (Chingelezi).