Mawu a M'munsi
a Liwu Lachigiriki logwiritsiridwa ntchito panopa, an·tiʹly·tron, silimapezeka kwina kulikonse m’Baibulo. Ilo nlogwirizana ndi liwu limene Yesu analigwiritsira ntchito kutanthauza dipo (lyʹtron) pa Marko 10:45. Komabe, The New International Dictionary of New Testament Theology imanena kuti an·tiʹly·tron ‘limapereka lingaliro la kusinthanitsa.’ Moyenerera, New World Translation imalimasulira kukhala “dipo lolinganira.”