Mawu a M'munsi
c Josephus analemba za zochitika pakati pa kuukira Yerusalemu koyamba kwa Aroma (66 C.E.) ndi chiwonongeko chake kuti: “Usikuwo kunaulika mkuntho wowononga; namondwe anawomba, mvula yamkokomo inagwa, mphezi zinang’anima mosalekeza, mabingu anagunda mochititsa mantha, dziko linanjenjemera ndi phokoso logonthetsa m’khutu. Tsoka la mtundu wa anthu linasonyezedweratu ndi kunyonyotsoka kwa mpangidwe wonse wa zinthu kumeneku, ndipo palibe aliyense amene anakayikira kuti zizindikirozi zinasonyeza tsoka lopanda lina lofanana nalo.”