Mawu a M'munsi
a Pamene kuli kwakuti Baibulo limanena kuti “chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta,” zimenezi sizimatanthauza kuti kuvutika kwa munthu kuli chilango cha Mulungu. (Agalatiya 6:7) M’dziko lolamulidwa ndi Satanali, kaŵirikaŵiri olungama amavutika kwambiri kuposa mmene amachitira oipa. (1 Yohane 5:19) “Adzada inu anthu onse chifukwa cha dzina langa,” Yesu anauza motero ophunzira ake. (Mateyu 10:22) Matenda ndi mitundu ina ya tsoka zingagwere atumiki a Mulungu okhulupirika alionse.—Salmo 41:3; 73:3-5; Afilipi 2:25-27.