Mawu a M'munsi
a Afarisi kwenikweni ndiwo anali ndi thayo la kuyambitsa mtundu wa Chiyuda chimene chiliko lerolino, chotero nkosadabwitsa kuti Chiyuda chimafunabe njira zozembera ziletso zake za Sabata zambiri zowonjezedwa. Mwachitsanzo, mlendo ku chipatala cha Ayuda amwambo pa Sabata angapeze kuti chikepe chimaima chokha pamalo alionse kuti okweramo asachite “ntchito” yauchimo ya kusinika batani ya chikepe. Madokotala ena achiyuda amalemba mapepala otengerapo mankhwala ndi inki imene imazimirira pambuyo pa masiku angapo. Chifukwa ninji? Mishnah imati kulemba ndi “ntchito,” koma imamasulira kuti “kulemba” ndiko kusiya chilembo chachikhalire.