Mawu a M'munsi
b Magazini yakuti Trost (Chitonthozo), yofalitsidwa ndi Watch Tower Society mu Bern, Switzerland, pa May 1, 1940, patsamba 10, inasimba kuti nthaŵi ina Mboni za Yehova zazikazi mu Lichtenburg sizinalandire chakudya chamasana masiku 14 chifukwa anakana kusonyeza chizindikiro chaulemu pamene nyimbo zotamanda Nazi zinali kuimbidwa. Mboni za Yehova pamenepo zinalipo 300.