Mawu a M'munsi
a Gulu la ku United States limeneli linasungabe miyambo ina yachipembedzo ya magulu ena akale achinsinsi mwa kugwiritsira ntchito mtanda umene ukupsa moto monga chizindikiro chake. Kalelo, gululi linali kuukira adani awo usiku, mamembala ake atavala mikanjo ndi nsalu zoyera ndi kufuzira mkwiyo wawo pa anthu akuda, Akatolika, Ayuda, anthu osakhala Aamereka, ndi mabungwe a antchito.