Mawu a M'munsi
c Kagulu kawo kanachokera kwa Ahasidi, gulu limene linakhalako zaka mazana ambiri kalelo kutsekereza chisonkhezero cha Agiriki. Ahasidi anatenga dzina lawo ku liwu lachihebri lakuti chasi·dhimʹ, kapena kuti “okhulupirika.” Mwina iwo ankaganiza kuti malemba omwe amatchula “okhulupirika” a Yehova anali kunena makamaka za iwo. (Salmo 50:5, NW) Iwowo, ndi Afarisi omwe anawatsatira, anadziika okha kutetezera zilembo za Chilamulo ndipo kukangalika kwawo kunali konkitsa.