Mawu a M'munsi
a Mabaibulo ena ndi zolembedwa zakale zachigiriki zimanena kuti Yesu anatuma ophunzira “makumi asanu ndi aŵiri mphambu aŵiri.” Komabe, pali umboni wokwanira wolembedwa wochirikiza “makumi asanu ndi aŵiri.” Kusiyana kumeneku kwa kaŵerengedwe sikuyenera kusokoneza mfundo yaikulu, yakuti Yesu anatumiza gulu lalikulu la ophunzira ake kukalalikira.