Mawu a M'munsi
c Kumene miyambo ya maliro ikhozadi kubweretsa chiyeso chachikulu pa Mkristu, akulu angakonzekeretse anthu ofuna ubatizo za zimene angakumane nazo. Pamene akukumana ndi achatsopano ameneŵa kuti akambitsirane nawo mafunso a m’buku la Olinganizidwa Kutsiriza Uminisitala Wathu, ayenera kupereka chisamaliro chapadera ku zigawo za “Moyo, Uchimo ndi Imfa” ndi “Kugwirizana Zipembedzo.” Zigawo zonsezi zili ndi mafunso odzisankhira a kukambitsirana. Akulu angagwiritsire ntchito mbaliyi kuti apereke chidziŵitso pa miyambo ya maliro yosemphana ndi Malemba kotero kuti munthu wofuna ubatizoyo angadziŵe zimene Mawu a Mulungu amafuna kwa iye ngati atayang’anizana ndi mikhalidwe yoteroyo.