Mawu a M'munsi
c M’buku lakuti History of the Jews, Polofesa Graetz ananena kuti nthaŵi zina Aroma anali kupachika akaidi 500 patsiku. Ayuda ena amene anatengedwa ukapolo anadulidwa manja kenako n’kuwabwezera kumzindawo. Kodi moyo unali wotani kumeneko? “Ndalama inatheratu mphamvu, popeza sinalinso kugula mkate. Amuna m’misewu anali kumenyanirana chakudya chonyansa kwadzaoneni, timapesi touma, kachikopa, kapena matumbo otayidwa kuti agalu adye. . . . Kuwonjezeka kwakukulu kwa mitembo yosaikidwa m’manda kunapangitsa mpweya wotentha wa m’chilimwewo kukhala ngati mliri, ndipo anthu ambiri anafa ndi matenda, njala, ndi lupanga.”