Mawu a M'munsi
a “Maopaleshoni olumikizanso [njira za ubwamuna], 40 peresenti mwa iwo amayenda bwino, ndipo pali umboni wosonyeza kuti ambiri adzayenda bwino njira zochitira maopaleshoni a ziwalo zing’onozing’ono zikamawongokera. Komabe, kutseketsa mwa amuna kuyenera kutengedwa kuti n’kwachikhalire.” (Encyclopædia Britannica) “Kutseketsa kuyenera kuonedwa kukhala kwachikhalire. Mosasamala kanthu kuti wotseketsayo wamvapo zotani ponena za kutsegulitsa, kulumikizanso njira zomwe zinadulidwa n’kodula, ndipo sungatsimikizire kuti kudzayenda bwino. Kwa akazi amene amakatsegulitsa, pamakhala ngozi yaikulu yakuti mimba n’kukhala m’malo olakwika.”—Contemporary OB/GYN, June 1998.