Mawu a M'munsi
b Lamulo lina limene lingaoneke kukhala latanthauzo linanena kuti mwamuna aliyense amene ziwalo zake zobalira zinawonongedwa kwambiri asaloŵe mumsonkhano wa Mulungu. (Deuteronomo 23:1) Komabe, Insight on the Scriptures imanena kuti lamulolo “linali kunena za kudzipundula dala ndi zolinga zakhalidwe loipa, monga kugonana kwa amuna kapena akazi okhaokha.” Chotero, lamulo limenelo silinali kunena za kufula kapena njira zolera za panthawiyo. Insight imanenanso kuti: “Motonthoza Yehova ananeneratu za nthaŵi pamene mifule idzalandiridwa ndi iye monga atumiki ake ndi kukhala ndi dzina loposa la ana aamuna ndi aakazi, ngati idzakhala yomvera. Chilamulocho chitathetsedwa ndi Yesu Kristu, anthu onse okhulupirira, mosasamala kanthu za zimene anali kuchita poyamba kapena mmene alili, anatha kukhala ana auzimu a Mulungu. Zinthu zakuthupi zosiyanitsa anthu zinachotsedwapo.—Yesaya 56:4, 5; Yohane 1:12.”