Mawu a M'munsi
a Buku lotchedwa Cyclopedia lolembedwa ndi McClintock ndi Strong limati: “Amsonkho otchulidwa m’Chipangano Chatsopano ankaonedwa monga akapirikoni ndi am’patuko, odetsedwa chifukwa cha kuyanjana kwawo nthaŵi zonse ndi anthu akunja, pokhala ziŵiya za opondereza. Anali kuwaika m’gulu limodzi ndi ochimwa . . . Posankhulidwa chotero ndiponso kupeŵedwa ndi anthu a moyo wabwino, mabwenzi awo okha kapena anzawo anali kupezeka pakati pa awo amene anali anthu okanidwa ofanana ndi iwo.”