Mawu a M'munsi
b Kuchita mwanzeru ndi mochenjera kwa Gideoni sikuyenera kulingaliridwa molakwa n’kumati chinali chizindikiro cha mantha. M’malo mwake, kulimba mtima kwakeko kwatsimikiziridwa pa Ahebri 11:32-38, pamene akutchula Gideoni limodzi ndi ena omwe “analimbikitsidwa” ndi amenenso “anakula mphamvu kunkhondo.”