Mawu a M'munsi
b Mwachitsanzo, kuti musinkhesinkhe mwapemphero chigawo cha m’Baibulo chimene mwaŵerenga, mungadzifunse kuti: ‘Kodi chikuonetsa khalidwe limodzi la Yehova kapena ambiri? Kodi zikugwirizana bwanji ndi mutu wa nkhani wa Baibulo? Kodi ndingachigwiritsire ntchito bwanji m’moyo wanga kapena pothandiza ena?’