Mawu a M'munsi
a Pofotokoza kawombezedwe ka panthawiyi, buku lakuti The Holy Bible, With an Explanatory and Critical Commentary, lolembedwa ndi F.C. Cook , linalongosola kuti: “Ankatero mwina poponya m’madzi golide, siliva, kapena mikanda kapenanso zibangili zamtengo wapatali n’kumaziyang’anitsitsa. Njira ina yachidule inali kungoyang’ana m’madzi ngati kuti akuyang’ana pa galasi.” Katswiri wina wa Baibulo Christopher Wordsworth anati: “Nthawi zina ankadzadza madzi m’chikho ndipo ankawombeza poyang’ana chithunzithunzi chopangidwa ndi dzuwa likamanyezimira m’madzi a m’chikhocho.”