Mawu a M'munsi
b Ngakhale kuti lemba la Mateyo 13:39-43 likunena mbali ina ya ntchito yolalikira Ufumu, nthawi ya kukwaniritsidwa kwake ndi nthawi yomwenso fanizo la khoka likukwaniritsidwa, yomwe ndi “pamapeto,” kapena kuti nthawi ino ya mathedwe “a dongosolo lino la zinthu.” Ntchito yolekanitsa nsomba zophiphiritsa ndi yochitika mopitiriza, monga mmene ntchito yofesa ndi kukolola ikupitirizira panthawi yonseyi.—Nsanja ya Olonda, October 15, 2000, masamba 25-26; Lambirani Mulungu Woona Yekha, masamba 178-181, ndime 8-11.