Mawu a M'munsi
b Baibulo la Septuagint limanena kuti Yona anagona tulo mpaka kufika poliza nkonono. Komabe tisaganize kuti Yona anagona chifukwa choti analibe nazo ntchito zimene zimachitikazo. Tisaiwale kuti anthu amatha kukhala ndi tulo kwambiri chifukwa cha nkhawa. Mwachitsanzo, panthawi imene Yesu anali pachipsinjo chachikulu kwambiri m’munda wa Getsemane, Petulo, Yakobe, ndi Yohane “anagona chifukwa cha chisoni.”—Luka 22:45.