Mawu a M'munsi
b Zikuoneka kuti Davide ankaona kuti kuteteza anthu a m’derali ndiponso ziweto zawo kunali kutumikira Yehova Mulungu. Masiku amenewo, m’derali munkakhala mbadwa Abulahamu, Isake ndi Yakobo chifukwa ndi zimene Yehova anakonza. Choncho ndi zoonadi kuti kuteteza anthu a m’derali ndiponso ziweto zawo unali utumiki wopatulika.