Mawu a M'munsi
a Mawu akuti “makala a moto” amanena za njira imene anthu ankagwiritsa ntchito poyenga zitsulo. Anthuwo ankaika makala a moto pamwamba ndi pansi pa chitsulo chimene akufuna kuyengacho. Tikamakomera mtima anthu amene atichitira zoipa, timafewetsa mtima wawo n’kuwathandiza kuti azisonyeza makhalidwe awo abwino.