Mawu a M'munsi
a Mawu amene amagwiritsa ntchito ponena za mabuku owonjezera a m’Baibulo (apocryphal) anachokera ku mawu achigiriki amene amatanthauza “kubisa.” Poyamba mawu amenewa ankanena za nkhani zimene zinkaphunzitsidwa pasukulu ina koma ankazibisa kuti amene saphunzira pasukulupo asazidziwe. Koma m’kupita kwa nthawi, mawuwa anayambanso kugwiritsidwa ntchito ponena za mabuku omwe sanaphatikizidwe m’gulu la mabuku ovomerezeka a m’Baibulo.