Mawu a M'munsi
a Anthu ena amanena kuti zikuoneka kuti Mulungu anachititsa nyama zonse kuti zikhale ngati zaulesi kapena ngati zagona n’cholinga choti zisamadye kwambiri. Kaya Mulungu anachitadi zimenezi kapena ayi, nkhani ndi yakuti anakwaniritsa lonjezo lake lakuti adzapulumutsa anthu ndi zinyama zomwe zinali m’chingalawamo.