Mawu a M'munsi
b Nyimbo ya Debora imasonyeza kuti nthawi zambiri Sisera akamachoka kunkhondo, ankabwerako ndi zinthu zosiyanasiyana komanso atsikana moti nthawi zina msilikali aliyense ankapatsidwa atsikana angapo. (Oweruza 5:30) Zikuoneka kuti atsikanawa ankawatenga kuti azigonana nawo basi ndipo pa nthawiyi ku Kanani azimayi ambiri ankagwiriridwa.