Mawu a M'munsi
c Nkhondoyi imafotokozedwa kawiri m’Baibulo. Koyamba inafotokozedwa ngati mbiri m’buku la Oweruza chaputala 4, kenako inafotokozedwa m’nyimbo imene Debora ndi Baraki analemba m’chaputala 5 cha buku lomweli. Nkhanizi n’zogwirizana koma iliyonse imafotokoza mfundo zina zomwe m’nkhani ina mulibe.