Mawu a M'munsi
a Mwachitsanzo, katswiri wina wolemba mbiri yakale, dzina lake Tacitus, yemwe anabadwa cha m’ma 55 C.E., analemba kuti: “Khristu, [dzina limene Akhristu anatengerako dzina lawo] anazunzidwa kwambiri ndi bwanamkubwa wathu Pontiyo Pilato, pa nthawi ya ulamuliro wa Mfumu Tiberiyo.” Palinso olemba mbiri ena a m’zaka 100 zoyambirira amene anachitira umboni za Yesu monga Seutonius ndi Josephus, wolemba mbiri wachiyuda. Zitatha zaka 100 zoyambirira, Pliny Wamng’ono yemwe anali bwanamkubwa wa mzinda wa Bituniya, nayenso analemba zokhudza Yesu.