Mawu a M'munsi
a Akatswiri ena a Baibulo amanena kuti uthenga wa Inoki umene Yuda analemba anautenga m’buku lakuti Buku la Inoki. Koma Yuda sakanatenga uthengawu m’bukuli chifukwa nkhani zambiri za m’bukuli ndi zongopeka komanso si zoona kuti linalembedwa ndi Inoki ndipo silikudziwika kumene linachokera. N’zoona kuti bukuli lili ndi uthenga wa Inoki koma mwina olemba ake anautenga m’zolemba zina zakale kapena anachita kuuzidwa ndi anthu ena. N’kutheka kuti uthenga wa Inoki umene Yuda analembawu anautenganso kumene olemba Buku la Inoki anatenga uthengawu. Apo ayi, mwina anamva kwa Yesu, yemwe anali kumwamba pamene Inoki anali ndi moyo.