Mawu a M'munsi
a Kaya takhala tikutumikira Yehova kwa nthawi yaitali bwanji, tonsefe timafunika kusinthabe zinthu zina kuti tikhale Akhristu abwino kwambiri. Mtumwi Paulo analimbikitsa Akhristu anzake kuti asabwerere m’mbuyo. M’kalata imene analembera Akhristu a ku Filipi, muli mfundo zimene zingatithandize kuti tipirire pa mpikisano wokalandira moyo. Munkhaniyi tikambirana zimene tingachite kuti titsatire malangizo a Paulo amenewa.