Mawu a M'munsi
a Tikudziwa kuti posachedwapa, padzikoli padzachitika “chisautso chachikulu.” Kodi n’chiyani chidzatichitikire ifeyo pa nthawiyo? Nanga kodi Yehova adzafuna kuti tidzachite chiyani? Kodi ndi makhalidwe ati amene tiyenera kuyesetsa kukhala nawo panopa n’cholinga choti tidzakhalebe okhulupirika? Munkhaniyi tipeza mayankho a mafunso amenewa.