Mawu a M'munsi
a Atumiki onse a Yehova amayesetsa kuwerenga Mawu ake tsiku lililonse. Anthu enanso ambiri amawerenga Baibulo koma samvetsa zimene amawerengazo. Ndi mmenenso zinalili ndi anthu ena mu nthawi ya Yesu. Kuona zimene Yesu anauza anthu amene amawerenga Mawu a Mulungu, kungatithandize kuphunzira zinthu zina zomwe zingatithandize kuti tizipindula kwambiri tikamawerenga Baibulo.