Mawu a M'munsi
a Yehova anatchula msewu wophiphiritsa wochoka ku Babulo kupita ku Isiraeli kuti “Msewu wa Chiyero.” Kodi masiku anonso Yehova wakonzera anthu ake msewu ngati umenewu? Inde. Kungochokera mu 1919, anthu mamiliyoni akhala akutuluka mu Babulo Wamkulu n’kuyamba kuyenda pa “Msewu wa Chiyero.” Tonsefe tiyenera kupitiriza kuyenda pamsewu umenewu mpaka tikafike kumene tikupita.