Mawu a M'munsi
b N’kutheka kuti panali zifukwa zitatu zomwe zinachititsa Danieli kuganiza kuti zakudya za ku Babulo zinali zodetsedwa: (1) Mwina nyama yomwe anapatsidwa inali m’gulu la nyama zoletsedwa m’Chilamulo. (Deut. 14:7, 8) (2) Kapenanso nyama yake inali yosazinga. (Lev. 17:10-12) (3) Kudya chakudyacho kukanaoneka ngati mbali yakulambira mulungu wonyenga.—Yerekezerani ndi Levitiko 7:15 ndi 1 Akorinto 10:18, 21, 22.