Mawu a M'munsi
f MAWU OFOTOKOZERA CHITHUNZI: Alongo awiri akupemphera kuti akalowe Sukulu ya Akhristu Olalikira za Ufumu. Mlongo mmodzi akuitanidwa kusukuluyo pomwe winayo sakuitanidwa. M’malo mokhumudwa, mlongo yemwe sanaitanidweyo akupempha Yehova kuti amuthandize kuzindikira mwayi wina wa utumiki. Kenako akulembera kalata ofesi yanthambi n’cholinga choti adziwe komwe kukufunikira olalikira ambiri.