Mawu a M'munsi
a Timafuna kuti Mulungu azisangalala nafe komanso azitiona kuti ndife olungama. Pogwiritsa ntchito zimene Paulo ndi Yakobo analemba, nkhaniyi itithandiza kuona kuti zimenezi ndi zotheka. Tionanso chifukwa chake chikhulupiriro ndi ntchito zili zofunika kuti Yehova azisangalala nafe.