Mawu a M'munsi
c Ndi cholinga cha Mulungu kuti anthu okwatirana azikhala limodzi kwa ndi moyo wawo wonse. Iye amalola anthu okwatirana kuthetsa banja lawo ndi kukwatirananso ndi munthu wina pokhapokha ngati wina wachita chigololo. (Mateyu 19:9) Ngati mukulimbana ndi mavuto am’banja, Baibulo lingakuthandizeni kuthana ndi mavutowo mwanzeru komanso mwachikondi.