Mawu a M'munsi
a Pamene nthawi inkapita, zinthu zina zinasintha. Mwachitsanzo, pamene Aisiraeli ankachita mwambo woyamba, anauzidwa kuti adzauchite “mofulumira” chifukwa ankafunika kukonzekera zochoka ku Iguputo. (Ekisodo 12:11) Komabe atafika ku Dziko Lolonjezedwa, Aisiraeli sankafunikanso kuchita zinthu mofulumira ngati poyamba.