Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Amuna ndi Akazi Kodi Amalankhuladi Mosiyana?
    Galamukani!—1994 | February 8
    • Amuna ndi Akazi Kodi Amalankhuladi Mosiyana?

      TINENE kuti Bill analoŵa mu ofesi ya Jerry modzikwakwaza, atazyolika mutu chifukwa cha nkhaŵa zake. Jerry anayang’anitsitsa mofatsa bwenzi lake namuyembekezera kuyamba kulankhula. “Sindikudziŵa ngati ndingathe kuchita pangano limeneli bwino lomwe,” anausa moyo motero Bill. “Pali zovuta zambiri, ndipo a ku ofesi yaikulu akundipanikiza.” “Kodi ukudandaula ndi chiyani, Bill?” Jerry mwachidaliro anafunsa motero. “Udziŵa kuti ndiwe munthu woyenerera kwambiri ntchitoyo, ndipo iwo amadziŵanso zimenezo. Ingodekha pang’ono. Kodi uganiza kuti limeneli ndivuto? Tangoganiza, mwezi wathawo . . . ” Jerry anasimba moseketsa za mmene vuto lake laling’ono linayendera ndipo posapita nthaŵi bwenzi lakelo linatuluka mu ofesiyo likuseka ndi lotonthozedwa. Jerry anali wachimwemwe kuti anathandiza.

      Ndiponso tinene kuti pamene anafika kunyumba madzulowo, Jerry anatha kuoneratu kuti mkazi wake, Pam, nayenso anali wosakondwa. Iye analonjera mkazi wakeyo mwachisangalalo chachikulu namuyembekezera kunena zimene zinamuvuta. Pambuyo pa kukhala duu kwakanthaŵi, analankhula mwaukali kuti: “Sindingapirirenso nazo! Bwana watsopanoyu ngwankhanza!” Jerry anamkhazika pansi, namgwira m’chuuno, nati: “Wokondedwa, usakwiyetu kwambiri. Taona, ndimo mmene ntchito iliri. Mabwana ngotero. Bwenzi ukanamva mmene wanga analankhulira mwaukali lero. Komabe, ngati ukuona kukhala zokuvuta kwambiri, ingoleka.”

      “Simukusamala mmene ndikumvera mpang’ono pomwe!” Pam anayankha modula mawu motero. “Simundimvetsera konse! Sindingaleke! Simumalandira ndalama zokwanira!” Pam anathamangira kuchipinda chogona kukalira kwambiri. Jerry anaima mwamantha kunja kwa chitseko chotsekedwa, akumadabwa chimene chinachitika. Kodi nchifukwa ninji panali machitidwe osiyana ndi mawu achitonthozo a Jerry otero?

      Kusiyana kwa Amuna ndi Akazi Kodi?

      Ena anganene kuti kusiyana kwa m’mafanizo ameneŵa kuli kaamba ka chenicheni chosavuta chakuti: Bill ndimwamuna; Pam ndimkazi. Akatswiri ofufuza malankhulidwe amakhulupirira kuti kaŵirikaŵiri zovuta za kulankhulana muukwati zimakhalapo chifukwa cha kusiyana kwa mwamuna ndi mkazi. Mabuku onga akuti You Just Don’t Understand ndi Men Are From Mars, Women Are From Venus amachirikiza lingaliro lakuti amuna ndi akazi, ngakhale kuti amalankhula chinenero chofanana, ali ndi njira zosiyana kwambiri za kulankhulana.

      Mosakayikira, pamene Yehova analenga mkazi kuchokera mwa mwamuna, mkaziyo sanali munthu woumbidwa mosiyana pang’ono. Mwamuna ndi mkazi analinganizidwa mosamalitsa ndi molingaliridwa bwino kuti athangatane—mwakuthupi, mwamalingaliro, mwamaganizo, mwauzimu. Wonjezerani pakusiyana kwachibadwa kumeneku maleredwe ocholoŵana a munthu ndi zokumana nazo za m’moyo ndi malingaliro a munthu oumbidwa ndi mwambo wa anthu, malo okhala, ndi lingaliro la chitaganya la zimene zili zachimuna kapena zachikazi. Chifukwa cha zisonkhezero zimenezi, kungakhale kotheka kudziŵa njira zina zimene amuna ndi akazi amalankhulirana. Koma “mwamuna weniweni” kapena “mkazi weniweni” wovuta kufotokozedwa angangopezeka kokha m’masamba a mabuku a phunziro la zaubongo ndi khalidwe.

      Akazi amadziŵidwa mwapadera chifukwa cha kutengeka kwawo maganizo msanga, komabe amuna ambiri ngochita zinthu ndi anthu ena mosamala kwambiri. Amuna angafotokozedwe kukhala olingalira mwanzeru kwambiri, komabe kaŵirikaŵiri akazi amakonda kupenda zinthu mwaluntha. Chotero pamene kuli kwakuti nkosatheka kutchula mkhalidwe uliwonse kukhala kalingaliridwe kachimuna kapena kachikazi chabe, pali chinthu chimodzi chotsimikizirika: Kudziŵa malingaliro a wina kungachite mbali yaikulu pakati pa kukhalitsana mwamtendere ndi kuvutana kotheratu, makamaka muukwati.

      Chitokoso cha tsiku ndi tsiku cha kulankhulana kwa amuna ndi akazi muukwati nchachikulu. Amuna ambiri ozindikira angachitire umboni wakuti funso looneka kukhala losavuta lakuti “Kodi mukuona bwanji kakonzedwe katsopano ka tsitsi langali?” lingakhale langozi. Akazi ambiri olankhula mwaluso amaphunzira kupeŵa kufunsa mobwerezabwereza kuti, “Bwanji osangofunsa msewu wake?” pamene amuna awo atayika poyenda ulendo. Mmalo mwa kupeputsa mikhalidwe yoonekera kukhala yosiyanayo ya wamuukwati wina ndi kuumirira gwagwagwa pamkhalidwe wako chifukwa chakuti “ndimo mmene ndiliri,” okwatirana achikondi amalingalira mwakuya. Kumeneku sikupenda mopambanitsa njira za wina ndi mnzake za kulankhulana koma kupendana mtima ndi maganizo mwachikondi kwa wina ndi mnzake.

      Monga momwe munthu aliyense aliri wosiyana ndi wina, choteronso ndi mgwirizano uliwonse wa anthu aŵiri muukwati. Kugwirizana kowona kwa maganizo ndi mitima sikumachitika mwamwaŵi koma kumafuna kukugwirira ntchito mwamphamvu chifukwa cha chibadwa chathu chaumunthu chosalungama. Mwachitsanzo, nkosavuta kulingalira kuti ena amaona zinthu monga momwe timachitira. Kaŵirikaŵiri timakwaniritsa zosoŵa za ena m’njira imene tikafuna kuti atichitire, mwinamwake mwa kuyesayesa kutsatira Lamulo la Makhalidwe Abwino lakuti, “Zinthu zilizonse mukafuna kuti anthu achitire inu, inunso muwachitire iwo zotero.” (Mateyu 7:12) Komabe, Yesu sanatanthauze kuti zimene mumafuna ziyenera kukhala zabwino mokwanira kwa ena. Mmalomwake, mumafuna kuti ena akapereke zimene muzisoŵa kapena kuzifuna. Chotero muyenera kupereka zimene amafuna. Zimenezi nzofunika makamaka muukwati, popeza kuti aliyense anawinda kukwaniritsa mokwanira monga momwe kungathekere zosoŵa za mnzake wa muukwati.

      Pam ndi Jerry anapanga chiwindo chotero. Ndipo mgwirizano wawo waukwati wa zaka ziŵiri wakhala wachimwemwe. Komabe, ngakhale kuli kwakuti iwo amalingalira kuti amadziŵana bwino kwambiri, nthaŵi zina pamabuka mikhalidwe imene imavumbula kusiyana kwakukulu kwa kulankhulana kumene kulipo kumene sikungathetsedwe ndi zolinga zabwino chabe. “Mtima wa wanzeru uchenjeza m’kamwa mwake,” pamatero pa Miyambo 16:23. Inde, kukhala ndi nzeru m’kulankhulana ndiko mfungulo yofunika. Tiyeni tione zimene nzeru imatsegulira Jerry ndi Pam.

      Lingaliro la Mwamuna

      Jerry akukhala m’dziko la m’malingaliro lampikisano mmene mwamuna aliyense ayenera kutetezera malo ake m’dongosolo la chitaganya, kaya akhale woyang’aniridwa kapena woyang’anira mumkhalidwe uliwonse. Kulankhulana amakugwiritsira ntchito kulimbitsira malo ake, kusonyeza kwake kukhoza, ukatswiri, kapena kufunika kwake. Kudziimira kwake payekha nkwamtengo wapatali kwa iye. Chotero pamene apatsidwa malamulo molamuliridwa, Jerry amangoona kuti akutsutsa. Uthenga wobisika wakuti “Sukuchita zimene uyenera kuchita” umampangitsa kutsutsa, ngakhale ngati pempho lake lili lanzeru.

      Jerry amakambitsirana ndi ena kwakukulu kuti asinthane chidziŵitso. Amakonda kulankhula za zinthu zowona, malingaliro, ndi zinthu zatsopano zimene waphunzira.

      Pamene akumvetsera, sikaŵirikaŵiri pamene Jerry amadula mawu wolankhula, ngakhale ndi mawu ovomereza onga akuti “aha, inde,” chifukwa chakuti amakhala akumvetsetsa chidziŵitsocho. Koma ngati sakugwirizana ndi zimene zanenedwa, iye sangazengereze kutsutsa, makamaka kwa bwenzi lake. Zimenezi zimasonyeza kuti iye ali wokondwerera zimene bwenzi liti linene, akumapenda kalikonse konenedwa.

      Ngati Jerry ali ndi vuto, amafuna kulithetsa yekha. Zikatero angachotse maganizo kwa aliyense ndi pachinthu chilichonse. Kapena iye angafune kutsitsimula maganizo ndi kanthu kena kuti aiŵale vutolo kwakanthaŵi. Iye adzakambitsirana vutolo ndi ena kokha ngati akufunafuna uphungu.

      Ngati munthu wina afika kwa Jerry ndi vuto monga momwe Bill anachitira, Jerry amazindikira kuti ndintchito yake kumthandiza, akumasamala kusapangitsa bwenzi lake kudziona kukhala losakhoza. Kaŵirikaŵiri amakambitsirana naye za mavuto ake ena limodzi ndi uphunguwo kotero kuti bwenzi lakelo lisaone kuti lili lokhalokha m’mavuto.

      Jerry amakonda kuchita zinthu pamodzi ndi mabwenzi. Utsamwali kwa iye umatanthauza kuchitira zinthu pamodzi.

      Kwa Jerry panyumba pamangokhala malo othaŵirako kuchoka kumalo ampikisano, ali malo kumene safunikiranso kulankhula zambiri kuti atsimikiziridwe, amene amalandiridwako, kudaliridwa, kukondedwa, ndi kuyamikiridwa. Ngakhale zili choncho, nthaŵi zina Jerry amaona kuti amafunikira kukhala ali yekha. Zimenezi zingakhale zilibe chochita ndi Pam kapena kanthu kena kalikonse kamene mkaziyo wachita. Iye amangofuna kudzipatula pang’ono. Jerry amapeza kukhala kovuta kuvumbula mantha ake, nkhaŵa zake, ndi mavuto kwa mkazi wake. Samafuna kumvutitsa maganizo. Thayo lake ndilo kumsamalira ndi kumtetezera, ndipo amafuna kuti Pam amdalire pochita zimenezi. Pamene kuli kwakuti Jerry amafuna chichirikizo, samafuna kumveredwa chisoni. Kumampangitsa kulingalira kukhala wosakhoza kuchita zinthu kapena wopanda pake.

      Lingaliro la Mkazi

      Pam amadziona kukhala munthu amene ali m’dziko lofuna kudalirana ndi ena. Kwa iye kukhazikitsa ndi kulimbitsa maunansi ameneŵa nkofunika. Kukambitsirana ndiko njira yofunika yolinganizira ndi kutsimikiziritsa kuyandikana.

      Kudalira munthu wina nkwachibadwa kwa Pam. Amalingalira kukhala wokondedwa ngati Jerry azindikira malingaliro ake asanapange chosankha, ngakhale kuti amafuna kuti iyeyo atsogolere. Pamene ayenera kupanga chosankha, amakonda kufunsa mwamuna wake, osati kwenikweni kuti amuuze chochita, koma kusonyeza kuyandikana kwake ndi kudalira pa iye.

      Nkovuta kwa Pam kutulukira poyera ndi kunena kuti akufuna kanthu kakutikakuti. Samafuna kuvutitsa Jerry kapena kumpangitsa kulingalira kuti alibe chimwemwe. Mmalomwake, amayembekezera kuzindikiridwa kapena amapereka malingaliro osonyeza zimenezo pang’onopang’ono.

      Pamene Pam akukambitsirana ndi munthu, amachititsidwa chidwi ndi zinthu zazing’ono ndipo amafunsa mafunso ambiri. Zimenezi nzachibadwa chifukwa cha kutengeka maganizo kwake msanga ndi kukondwerera anthu kwakukulu ndi maunansi.

      Pamene Pam akumvetsera, amaloŵerera m’mawu a wolankhula akudabwa, kugwedezera mutu, kapena akufunsa mafunso kusonyeza kuti akutsatira wolankhulayo ndipo akusamalira zimene ati anene.

      Amayesayesa mwamphamvu kuzindikira mwachibadwa zimene anthu akufunikira. Kupereka chithandizo mosapemphedwa ndiko njira yabwino kwambiri kwa iye yosonyezera chikondi. Iye amafuna makamaka kuthandiza mwamuna wake kukula m’maganizo ndi kuwongolera zinthu.

      Pamene Pam ali ndi vuto, angadzione kukhala wothedwa nzeru. Iye ayenera kulinena, kwenikweni osati kuti apeze yankho lake, koma kusonyeza malingaliro ake. Afuna kudziŵa kuti munthu wina amamvetsetsa ndipo amasamala. Pamene ali wokwiya, Pam amalankhula mokhadzula mawu. Iye samatanthauza kwenikweni zimenezo pamene amati: “Simumandimvetsera konse!”

      Bwenzi la Pam paubwana wake silinali lija limene anachita nalo zinthu pamodzi koma limene anakambitsirana nalo pafupifupi zinthu zonse. Chotero muukwati iye sali wokondweretsedwa kwambiri ndi zochitachita koma munthu womvetsera wachifundo amene angamuuze malingaliro ake.

      Panyumba mpamalo amene Pam angathe kunena zinthu popanda kuweruzidwa. Iye samazengereza kuvumbula mantha ake ndi mavuto kwa Jerry. Ngati akufuna chithandizo, samachita manyazi kuchipempha, pakuti amadalira kuti mwamuna wake alipo kuti amthandize ndipo amamvetsera.

      Kaŵirikaŵiri Pam amaona kukhala wokondedwa ndi wosungika muukwati wake. Koma panthaŵi zina, popanda chifukwa chenicheni, amayamba kudziona kukhala wopanda chitetezo ndi wosakondedwa ndipo amafuna chitsimikiziro chamwamsanga ndi ubwenzi.

      Inde, Jerry ndi Pam, othangatanawo, ngosiyana kwambiri. Kusiyana kumene kuli pakati pawo kumachititsa kuthekera kwa kusamvetsetsana kwakukulu, ngakhale kuti onsewo angakhale ndi zolinga zabwino koposa za kukhala okondana ndi ochirikizana. Ngati tikanamva lingaliro la aliyense wa iwo amene atchulidwa mumkhalidwe wa pamwambapawu, kodi akanenanji?

      Zimene Analingalira

      “Pamene ndinangofika panyumba, ndinatha kuona kuti Pam anali wosakondwa,” Jerry akananena motero. “Ndinalingalira kuti pamene adzakhala wokonzekera, adzandiuza chifukwa chake. Vutolo silinaonekere kukhala lalikulu kwambiri kwa ine. Ndinalingalira kuti ngati nditamthandiza kuona kuti sanafunikire kukwiya kwambiri ndi kuti vutolo linali losavuta kuthetsa, akanapeza bwinopo. Zinandivutitsadi maganizo, pamene ndinamvetsera akunena kuti, ‘Simumandimvetsera konse!’ Ndinalingalira monga ngati kuti anali kundiimba mlandu chifukwa cha kukhumudwitsidwa kwake konseko!”

      “Tsiku lonse linali lovuta kwambiri,” Pam akanafotokoza motero. “Ndinkadziŵa kuti sichinali chifukwa cha Jerry. Koma pamene anafika panyumba mumkhalidwe wachimwemwe, ndinalingalira kuti anali kunyalanyaza kuti ndinali wosakondwa. Nchifukwa chiyani sanandifunse chimene chinalakwika? Pamene ndinamuuza za vutolo, zimene anandiuza zinatanthauza kuti ndinali wopusa, kuti nkhaniyo inali yaing’ono. Mmalo mwa kunena kuti anazindikira mmene ndinamvera, Jerry, wothetsa mavutoyo, anandiuza mmene ndingathetsere vutolo. Sindinafune zothetsera mavuto, ndinkafuna kumveredwa chisoni!”

      Mosasamala kanthu za kusagwirizana kwakanthaŵi kumeneku kochitika panthaŵi ndi nthaŵi, Jerry ndi Pam amakondana kwambiri. Kodi ndiluntha lotani limene lidzawathandiza kusonyeza chikondi chimenechi bwino lomwe?

      Kuonera m’Lingaliro la Wina ndi Mnzake

      Jerry analingalira kuti kukakhala kududukira kufunsa Pam chimene chinalakwika, chotero mowona mtima iye anachitira Pam zimene iye akanafuna kuti ena amchitire. Anamuyembekezera kuti akhale womasuka ndi kuyamba kulankhula. Tsopano Pam anali wosakondwa osati kokha ndi vutolo komanso chifukwa chakuti Jerry anaonekera kukhala akunyalanyaza pempho lake lomchirikiza. Sanaone kukhala chete kwake monga chisonyezero cha kuchitira ulemu kwachikondi—anakuona monga kusasamala. Potsirizira pake pamene Pam analankhula, Jerry anamvetsera popanda kudodometsa. Koma Pam analingalira kuti iye kwenikweni sanali kumvetsera malingaliro ake. Ndiyeno mwamunayo anapereka chothetsera vutolo, osati kumvera chisoni. Zimenezi kwa iye zinatanthauza kuti Jerry anali kunena kuti: ‘Malingaliro akowo ngopanda pake; ukulingalira zinthu mopambanitsa. Kodi ukuona mmene vuto laling’ono limeneli liliri losavuta kulithetsa?’

      Zinthu zikanakhala zosiyana chotani nanga ngati aliyense wa iwo anali wokhoza kuona lingaliro la wina! Nkhaniyo ikanayenda motere:

      Jerry afika panyumba napeza Pam wosakondwa. “Chavuta nchiyani, wokondedwa?” iye akufunsa mwaulemu. Misozi ikuyamba kugwa, ndipo akufotokoza vuto lake lonse ndi mtima wonse. Pam sakunena kuti, “Nchifukwa chako!” kapena kupereka lingaliro lakuti Jerry sakusamala kwenikweni. Jerry amkupatira namvetsera moleza mtima. Pamene wamaliza, Jerry akuti: “Pepa kuti ukuvutika maganizo. Ndikuona chifukwa chimene uliri wosakondwa motere.” Pam akuyankha kuti: “Zikomo kwambiri chifukwa cha kumvetsera. Ndikumva bwino tsono kudziŵa kuti mukudziŵa zimenezi.”

      Mwachisoni, mmalo mwa kuthetsa bwino mkangano, a muukwati ambiri amangosankha kuthetsa ukwati wawo mwa chisudzulo. Kusoŵeka kwa kulankhulana ndiko mpalu amene amaononga maukwati ambiri. Pamabuka mikangano imene imagwedeza maziko enieniwo a ukwati. Kodi zimenezi zimachitika motani? Nkhani yotsatira ikufotokoza mmene zimenezi zimachitikira ndi mmene zingapeŵedwere.

  • Kupenda Zochititsa Mkangano
    Galamukani!—1994 | February 8
    • Kupenda Zochititsa Mkangano

      MKAZI amafuna kusonyeza mmene amamvera. Mwamuna amafuna kupereka zothetsera mavuto. Mikangano mamiliyoni ambiri ya muukwati kuyambira kalekale yakhala yosiyanasiyana, koma kaŵirikaŵiri pakhala zifukwa zake zazikulu zochititsa zosiyanasiyana. Kuzindikira malingaliro kapena njira yolankhulana yosiyana ya mnzanu wa muukwati kungathandize kuchepetsa moto wolirima wotentha nkhalango umenewu kukhala moto wofunditsa m’nyumba yachimwemwe.

      “Usalamulire Moyo Wanga!”

      Mawu ofananawo onenedwa mosalekeza a mkazi wokonda kulamulira, wovutitsa, angavutitse banja akumapangitsa amuna ambiri kukhala oletsedwa kwambiri ndi uphungu, mapempho, ndi zisulizo. Baibulo limasonyeza malingaliro otero, kuti: “Makangano a mkazi ndiwo kudonthadonthabe.” (Miyambo 19:13) Mkazi angapereke pempho limene mwamuna wake angalitsutse mwakachetechete pazifukwa zosadziŵika kwa mkaziyo. Poganiza kuti sanamve, iye tsono akumuuza zimene ayenera kuchita. Kukana kwake kukukhala kwamphamvu. Kodi ndiwo mkazi wovutitsa ndi mwamuna wouma khosi? Kapena kodi angokhala anthu aŵiri osakhoza kulankhulana bwino?

      M’lingaliro la mkaziyo, iye amasonyeza chikondi chake bwino koposa kwa mwamuna wake pamene apereka uphungu wothandiza. M’lingaliro la mwamuna wake, mkaziyo akumlamulira ndipo akupereka lingaliro lakuti iye ngwosakhoza kuchita zinthu. “Musaiŵale chola chanu” ndiwo mawu osonyeza kusamala kwake, otsimikizira kuti wanyamula zonse zomwe afunikira. Mawuwa amakumbutsa mwamunayo za amake akumafuula kwa iye pakhomo kuti, “Kodi watenga juzi yako?”

      Mkazi amene watopa anganene mwaulemu kuti, “Kodi mukufuna kukadyera kulesitiranti madzulo ano?” kwenikweni akumatanthauza kuti, “Kodi simumka nane kukadya kulesitiranti lero madzulo? Sindingathe kuphika chifukwa ndatopa.” Koma mwamuna wake wachikondiyo angagwiritsire ntchito mpata umenewu kuyamikira zomwe amaphika ndi kunenetsa kuti amazikonda kuposa zina zilizonse. Kapena angalingalire kuti, ‘Mkaziyu akuyesa kundilamulira mochenjera!’ Zidakali choncho, mkaziyo moipidwa anganene mumtima kuti, ‘Aa, kodi ndimafunsiranji?’

      “Simundikonda!”

      “Kodi angalingalire zimenezo motani?” akutero mwamuna wogwiritsidwa mwala ndi wovutika maganizo. “Ndimagwira ntchito, kupereka ndalama zolipirira zinthu, ndi kumbweretsera ngakhale maluŵa nthaŵi zina!”

      Pamene kuli kwakuti anthu onse amafuna kukondedwa, mkazi amafuna kutsimikiziridwa mwapadera zimenezi ndi mobwerezabwereza. Iye sanganene zimenezi momvedwa, koma mumtima mwake amamva monga chothodwetsa, makamaka pamene nthaŵi yake ya kusamba ikumchititsa kukhala wotsenderezeka maganizo. Panthaŵi zotero mwamuna wake angatalikirane naye, akumaganiza kuti mkaziyo akufuna nthaŵi yoti akhale yekha. Mkaziyo angaone kutalikirana naye kwa mwamunayo monga chitsimikiziro cha nkhaŵa yake yaikuluyo—yakuti samamkondanso. Angamlalatire, akumayesayesa kumuumiriza kumkonda ndi kumchirikiza.

      “Kodi Chavuta Nchiyani, Wokondedwa?”

      Njira yosamalira vuto lopsinja maganizo ya mwamuna ingakhale ya kupeza malo abata kuti alisinkhesinkhe. Mkazi angazindikire mwachibadwa kuti pali vuto nasonkhezereka kuchitapo kanthu mwa kuyesa kumchititsa kuti alankhulane. Komabe mulimonse mmene zoyesayesa zimenezi zingakhalire zabwino, mwamuna angazione kukhala mkhalidwe wa kududukira ndi womchititsa manyazi. Pamene akudzipatula kuti asinkhesinkhe za vuto lake, akuyang’ana kumbuyo ndi kuona mkazi wake wokhulupirikayo akumlondola mosalekeza. Mwamunayo akumva liwu lachikondi losalekezalo: “Kodi muli bwino wokondedwa? Chavuta nchiyani? Tiyeni tikambitsirane.”

      Ngati palibe yankho, mkaziyo angavutike mtima. Pamene ali ndi vuto, mkaziyo amafuna kukambitsirana za ilo ndi mwamunayo. Koma mwamuna amene amakondayo sakufuna kukambitsirana naye malingaliro ake. “Sakundikondanso” iye angagamule motero. Chotero pamene mwamuna wosazindikirayo achoka mumkhalidwe wake wodzipatulawo, wokhutiritsidwa ndi chothetsera vuto chimene wapeza, amapezanso, osati mnzake wa muukwati wachikondi amene anamsiya, koma mkazi wokwiya wokonzekera kumuimba mlandu chifukwa cha kumsiya yekhayekha.

      “Simumandimvetsera Konse!”

      Chinenezo chimenechi chimaonekera kukhala choseketsa. Kwa mwamunayo kumaonekera monga ngati kuti zomwe ayenera kuchita ndizo kumvetsera basi. Koma pamene mkazi wa mwamunayo akulankhula, mkaziyo amakhala akulingalira mwapadera kuti mawu ake akutengedwa ndi kupendedwa ndi kompyuta yoŵerengera masamu. Zikayikiro zake zimatsimikiziridwa pamene, mkati mwa kulankhula kwake, mwamunayo molanda mawu anena kuti: “Chabwino, bwanji osango . . . ?”

      Pamene mkazi adza kwa mwamuna wake ndi vuto, kaŵirikaŵiri samamuimba mlandu kapena kudzafunafuna yankho kwa iye. Chimene amafuna kwambiri ndicho munthu amene adzamumvetsera momvera chisoni, osati pa zenizeni zokha, koma malingaliro a mkaziyo pa izo. Ndiyeno amafuna, osati uphungu, koma kuvomerezedwa kwa malingaliro ake. Nchifukwa chake kaŵirikaŵiri mwamuna wokhala ndi cholinga chabwino amabutsa mkangano kokha pamene anena kuti: “Usalingalire choncho, wokondedwa. Imeneyo sinkhani yaikulu kwambiri.”

      Kaŵirikaŵiri, anthu amayembekezera anzawo a muukwati kudziŵa zimene akuganiza. “Takhala muukwati kwa zaka 25,” mwamuna wina anatero. “Ngati sakudziŵa zimene ndimafuna kufikira tsopano lino, ndiye kuti sasamala kapena samvetsera.” Wolemba mabuku wina m’buku lake akunena za maunansi a ukwati kuti: “Pamene anthu a muukwati sauzana zimene akufuna ndi kusulizana mosalekeza chifukwa cha kuphonya mpata wochitira zinthu, nkosadabwitsa kuti mzimu wachikondi ndi kugwirizana zimazimiririka. Mmalo mwake mumadza . . . mpikisano umene wa muukwati aliyense amayesayesa kuumiriza wina kukwaniritsa zofuna zake.”

      “Ndinu Wosasamala!”

      Mwina mkazi sanganene zimenezo mwachindunji kwa mwamuna wake, koma angapereke lingaliro lake moonekera bwino kwambiri m’kamvekedwe ka liwu lake. Mawu akuti “Kodi mwachedweranji kwambiri chotere?” angaonekere kukhala ofuna mafotokozedwe. Komabe, mwachionekere kwambiri, kayang’anidwe kake koimba mlandu dzanja lili m’chuuno kamanena kwa mwamuna wake kuti: “Kamwana kosasamala iwe, wandivutitsa maganizo. Chifukwa ninji sunandiimbire foni? Ndiwe wosalingalira bwino eti! Taona tsopano wawonongetsa chakudya!”

      Zowonadi, iye ngwolondola ponena za chakudya. Koma ngati pabuka mkangano, kodi unansi wawonso ungakhale pachiswe? “Mikangano yambiri imachitika osati chifukwa chakuti anthu aŵiri sakugwirizana, koma chifukwa chakuti mwina mwamuna akulingalira kuti mkazi sakuvomereza lingaliro lake kapena chifukwa chakuti mkazi sakuvomereza mmene akulankhulirana naye,” akutero Dr. John Gray.

      Ena ali ndi malingaliro akuti munthu ayenera kukhala womasuka kunena chilichonse chimene akufuna panyumba. Koma munthu wodziŵa bwino kulankhulana amafunafuna mgwirizano ndi kubweretsa mtendere, akumalingalira malingaliro a womvetsera. Tingayerekezere mwawamba kulankhulana kotero ndi kupatsa mnzanu wa muukwati tambula ya madzi ozizira mosiyana ndi kumuwaza nawo kumaso. Tinganene kuti kusiyana kwake kuli m’kaperekedwe.

      Kugwiritsira ntchito mawu a pa Akolose 3:12-14 kudzachotsa mikangano ndi kudzetsa moyo wa banja wachimwemwe: “Valani . . . mtima wachifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, chifatso, kuleza mtima; kulolerana wina ndi mnzake, ndi kukhululukirana eni okha, ngati wina ali nacho chifukwa pa mnzake; monganso [Yehova, NW] anakhululukira inu, teroni inunso; koma koposa izi zonse khalani nacho chikondano, ndicho chomangira cha mtima wamphumphu.”

      [Chithunzi patsamba 25]

      Mwamuna akunena zinthu mochirikiza umboni, mkazi akunena zinthu mochirikiza malingaliro

  • Nyumba Yachimwemwe Imene Anthu Aŵiri Ali Ogwirizana
    Galamukani!—1994 | February 8
    • Nyumba Yachimwemwe Imene Anthu Aŵiri Ali Ogwirizana

      NGATI munafuna kumanga nyumba yolimba, yachisungiko, yabwino, kodi mukanagwiritsira ntchito zinthu zotani? Mitengo? Njerwa? Miyala? Nazi zimene buku la Baibulo la Miyambo limalangiza: “Nzeru imangitsa nyumba; luntha liikhazikitsa. Kudziŵa kudzaza zipinda zake ndi chuma chonse chofunika cha mtengo wake.” (Miyambo 24:3, 4) Inde, pamafunika nzeru, luntha, ndi chidziŵitso kuti timange nyumba yachimwemwe.

      Kodi ndani amene amamanga nyumbayo? “Mkazi yense wanzeru amanga banja lake; koma wopusa alipasula ndi manja ake.” (Miyambo 14:1) Zimenezi zili chonchonso kwa mwamuna wanzeru amene amaona kuti ndi manja ake akhoza kupangitsa ukwati wake kukhala wolimba ndi wachimwemwe kapena wofooka ndi wovuta. Kodi nzinthu zotani zimene zimapangitsa kusiyanako? Nkokondweretsa chotani nanga kuti malingaliro ena a alangizi amakono ngogwirizana kwambiri ndi nzeru yogwira ntchito panthaŵi iliyonse ya Mawu a Mulungu, yolembedwa zaka zikwi zambiri zapitazo.

      Kumvetsera: “Kwenikweni kumvetsera ndiko chimodzi cha zinthu zofunika kopambana zimene mungapereke kwa munthu wina ndipo nkofunika koposa m’kumanga ndi kusunga unansi wapafupi,” likutero buku lina la ukwati. “Khutu la anzeru lifunitsa kudziŵa,” imatero Miyambo. (Miyambo 18:15) Popeza kuti makutu otseguka ali osaoneka monga maso kapena pakamwa potseguka, kodi mungasonyeze motani wa muukwati mnzanu kuti mukumvetsera mowona mtima? Njira ina ndiyo mwa kulabadira, kapena kumvetsera kosamala.—Onani bokosi patsamba 27.

      Kumasuka ndi kuyandikana: “Mwambo wathu umatsutsa kumasuka,” likutero buku lakuti One to One—Understanding Personal Relationships. “Timaphunzitsidwa kusamala za munthu mwini kuyambira pausinkhu waung’ono—kukhala achinsinsi ponena za ndalama, njira zochitira zinthu, zolinga za mtima, . . . kanthu kalikonse kaumwini. Phunziro limeneli silimatha, ngakhale pamene ‘tikondana ndi munthu wina.’ Pokhapokha ngati kumenyera nkhondo kaamba ka kumasuka kopitirizabe kuchitika, kuyandikana sikungakhalepo.” “Zolingalira zizimidwa popanda upo,” imatero Miyambo, “koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.”—Miyambo 13:10; 15:22.

      Kukhulupirika ndi chidaliro: Mwamuna ndi mkazi amawinda pamaso pa Mulungu kukhala okhulupirika. Pamene okwatirana adalira kuti aliyense ali ndi thayo la kusamalira mnzake, chikondi chawo chimakhala chopanda chikayikiro, kunyada, mzimu wampikisano, kutanganitsidwa ndi zimene munthu akulingalira kukhala zomuyenerera.

      Kugaŵana: Unansi umakula ndi zokumana nazo zowoneredwa pamodzi. Pamene nthaŵi ipita anthu okwatiranawo angathe kupanga mbiri yogwirizana kwambiri imene aliyese amaŵerengera. Kulingalira zodula chomangira cha ubwenzi chimenecho ndiko kanthu kapatali ndi maganizo awo. “Lilipo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.”—Miyambo 18:24.

      Kukoma mtima ndi kufeŵa: Machitidwe okoma mtima amachepetsa mikangano ya m’moyo ndi kuthetsa kunyada. Njira za kukoma mtima, ngati zikhomerezeka, zimakhalapobe ngakhale ngati pakhala kukwiya mkati mwa kusagwirizana, motero kukumachepetsa chivulazo. Mkhalidwe wa kufeŵa umadzetsa mkhalidwe wachikondi mmene chikondi chimakula. Ngakhale kuti chifatso chingakhale chovuta makamaka kwa mwamuna kuchisonyeza, Baibulo limati: “Chotikondetsa munthu ndicho kukoma mtima kwake.” (Miyambo 19:22) Ponena za mkazi wabwino, “chilangizo cha chifundo chili palilime lake.”—Miyambo 31:26.

      Kudzichepetsa: Mankhwala othetsera vuto la kunyada, kudzichepetsa kumasonkhezera kukhala wokonzekera kupepesa ndi kuthokoza kaŵirikaŵiri. Bwanji nanga ngati mulidi wosalakwa pachokhumudwitsa chonenedwacho? Bwanji osangonena mwaulemu kuti, “Pepani kuti mwakwiya kwambiri”? Sonyezani nkhaŵa pamalingaliro a mnzanuyo, ndiyeno lingalirani pamodzi mmene mungawongolerere cholakwacho. “Kuli ulemu kwa mwamuna kupeŵa ndewu.”—Miyambo 20:3.

      Ulemu: “Liwu lofunika m’kuzindikira kusiyana maganizo kwa wina ndi mnzake ndi kukuthetsera pamodzi ndilo ulemu. Chinthu chimene chili chofunika kwa wina sichingakhale chofunika mofananamo kwa mnzake. Komabe, wa muukwati aliyense nthaŵi zonse akhoza kulemekeza malingaliro a wina.” (Keeping Your Family Together When the World Is Falling Apart) “Kudzikuza kupikisanitsa; koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.”—Miyambo 13:10.

      Nthabwala: Mkhalidwe wovuta kwambiri ungazimiririke mwa kusekera pamodzi. Kumalimbitsa chomangira cha chikondi ndi kuchepetsa mkangano umene kaŵirikaŵiri umawononga kuganiza kwabwino. “Mtima wokondwa usekeretsa nkhope.”—Miyambo 15:13.

      Kupatsa: Funafunani mwakhama zinthu zimene mungayamikire kwa mnzanu ndi kuthokoza ndi mtima wonse. Zinthu zokhumbika zimenezi zingachititse mtima kulabadira mokulirapo koposa taye wa silika kapena tsadzi la maluŵa. Zowonadi, mungathe kugulabe kapena kuchita zinthu zabwino kwa wina ndi mnzake. Koma “mphatso zazikulu koposa zimene mungapereke,” likutero buku lakuti Lifeskills for Adult Children, “sizingaikidwe m’bokosi. Ndizo kusonyeza chikondi kwanu ndi chiyamikiro, chilimbikitso chanu, ndi chithandizo chanu.” “Mau oyenera apanthaŵi yake akunga zipatso zagolidi m’nsengwa zasiliva.”—Miyambo 25:11.

      Ngati mikhalidwe imeneyi ingayerekezeredwe ndi njerwa zomangira unansi waukwati, pamenepo kulankhulana ndiko simenti yozigwirizanitsa pamodzi zolimba. Chotero, kodi nchiyani chimene okwatirana angachite pamene mikangano ibuka? “Mmalo mwa kuona malingaliro a mnzanu osiyanawo monga magwero a mkangano, . . . aoneni monga magwero a chidziŵitso. . . . Zochitika za moyo watsiku ndi tsiku zimakhala magwero a chuma cha chidziŵitso,” likutero buku lakuti Getting the Love You Want.

      Pamenepo, onani nthaŵi iliyonse ya mkangano, osati monga kuputana kuti mumenyane, koma monga mpata wamtengo wapatali wa kupeza chidziŵitso mwa munthu ameneyu amene mumakonda. Landirani pamodzi chitokoso cha kuthetsa kusiyana kumeneko ndi kufika pakugwirizana bwino lomwe, motero mukumalimbitsa zomangira, kukulitsa chikondi chimene chimapangitsa aŵirinu kukhala ogwirizana.

      Yehova Mulungu amaona kukongola kwakukulu m’kugwirizana kwa zinthu ndipo motero anakuika m’chilengedwe chake—m’kayendedwe ka okosijeni imene imatulutsidwa ndi kuloŵetsedwa m’zomera ndi nyama, kuzungulira kwa makamu akuthambo, maunansi a kukhalira limodzi kwa tizilombo ndi maluŵa. Choteronso, mumgwirizano waukwati, mungakhale kayendedwe ka zinthu kokondeka kamene mwamuna, m’mawu ndi machitidwe, amatsimikiziritsa mkazi wake za chikondi chake ndi chidaliro, mkazi wachikondi akumatsatira kutsogolera kwake mokhutira. Motero, aŵiriwo amakhaladi amodzi, akumadzetsa chisangalalo kwa wina ndi mnzake ndi kwa Woyambitsa ukwati, Yehova Mulungu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena